Ziyaratu Ashura 3

Ziyaratu Ashura 3
Imam  Swadiq (a)  pofuna  kulankhula  za  mavuto  amenewa  adanena  kuti:
إنّ  يوم عاشورا  أحرق قلوبنا  و أرسل  دموعنا و أرض  كربلا أورثتنا  الكرب  والبلاء  فعلى  مثل  الحسين  فليبك  الباكون  فإنّ  البكاء  عليه  يمحو الذنوب  أيّها  المؤمنون.
 Ndithudi  tsiku  la Ashura (tsiku lomwe  Imam  Husain(a) adaphedwa)  limaotcha  mitima  yathu,  limaketsa  misozi  yathu,    ife  tidalandira  madandaulo  ndi  mavuto  a Karibala  pachifukwachi  anthu  olira  ayenera  kulilira   Husain   chifukwa   kulilira  Husain  kumafufuta  zochima  za  munthu  e!  inu  anthu  okhulupirira  dziwani  zimenezi.
Naye  Imam  Ridtha  (a)  adanena  kuti: 
إنّ  يوم الحسين  أقرح جفوننا  و أسبل  دموعنا و أذلّ عزيزنا بأرض  كربلا....على مثل الحسين (ع)    فليبك  الباكون  فإنّ  البكاء  عليه  يحط العظام.  
Kuphedwa  kwa  Imam  Husain (a)  kudapweteka   maso  athu,  kudagwetsa  misozi  yathu  ndipo  munthu  amene  ali  olemekezeka  wathu  adachepetsedwa  pa  Karibala,   choncho  anthu  ayenera  kumulilira  Imam  Husain(a)  chifukwa  kumulilira  iye  kumachotsa   machimo  akuluakulu.
Munthu  wina  otchedwa  Abdullah  bin  Fudthail  Hashimi  adamufunsa  Imam   Swadiq (a)  kuti:  ndichifukwa  chani  kuti  tsiku  la  Ashura  lidasanduka  tsiku  la madandaulo,  mavuto  ndi   mazunzo  pomwe  tsiku  lomwe  Mtumiki(s.a.a.w),  Ali(a),  Fatwimah (a)   ndi  Hasan(a)  sizili  chonchi kumachita  kuti  nawonso  adaphedwa  modandaulitsa  pothiridwa  mankhwala  muzakudya  kapena  zakumwa? Imam  adayankha  kuti:  zili  chonchi  chifukwa  choti  kuphedwa  kwa  Imam  Husain (a)  tsiku la  Ashura  tikakufanizira  ndikuphedwa  kwa  ena  onse  omwe  atchulidwawa  tipeza  kuti  tsiku  limeneli  la  Ashura   ndi lalikulu kuposa  masiku  ena  onse  potengeranso  kakhalidwe  ka  mavuto  ake,  chifukwanso  choti  Imam  Husain (a)  ndi munthu  yemwe  adatsalira  mwa  anthu  asanu  omwe  amatchedwa  kuti  “Aswihabul  kisai” ndiye  kuphedwa  ndikusowa  kwa  iye  zidali ngati  kusowa  kwa  anthu onsewa.
Inde,  munthu  akakhala  ndikuganizira  mozama  mavuto  omwe  adachitika  ku Karibala  kuyambira  tsiku  loyamba  mpaka  lomaliza   popanda  kukhala  ndi mtima  wa  sankho  muchipembedzo  adzavomereza  kuti  kuphedwa  kwa  Imam  Husain (a)  idali  nkhani  ndi  mavuto  akulu  muchisilamu. 
M’bale  olemekezeka  muchipembedzo  cha  chisilamu,  kodi  mudziwa  kuti  munthu  Msilamu  ali  okakamizidwa  kuchita  kafukufuku  muchipembedzo  chimenechi  cha  chisilamu?  Pomwe  Mtumiki(s.a.a.w)  akunena  kuti:  Kufunafuna  maphunziro  ndichikakamizo  kwa  Msilamu  wina  aliyense  wamwamuna  ndi  wamkazi  yemwe.
Choncho  ngati  munthu  akufuna  kudziwa  zambiri  za nkhani  imeneyi  ya kuphedwa  kwa  Husain bin  Ali  bin Abi Twalib  yemwe  ndi  chidzukulu  cha Mtumiki  olemekezeka  cholonjezedwa  kukalowa  ku mtendere, ayenera  kuchita  kafukufuku  pa nkhaniyi. 
Komanso  ngati  munthu  sangakhale  ndi mpata  okwanira  atha  kukwaniritsidwa  ndi  “Site” imeneyi  chifukwa  mmenemu  tikhale  tikunena  zambiri  za  nkhaniyi  kapena  inu  mutha  kutidziwitsa   kuti  tinenepo  zambiri  pankhaniyi.
Mulungu  azikudalitsani  nthawi  zonse.
Wassalam alaikumu warahamatullah ta’ala  wabarakatuh wamaghafiratuh.

 

Add new comment