Zoyenera kupanga tsiku la chisangalalo chachikulu cha Mulungu cha Ghadir

 

Zoyenera  kupanga  tsiku la chisangalalo  chachikulu cha Mulungu  cha Ghadir
Ife  amathihabu  a Imamiyyah (Shia)  timakhulupirira  kuti  tsiku la pa  18 dthul hijah  ndilachisangalalo  pomwe  timakumbukira  kuti  nditsiku  lomwe  Mtumiki  wathu  olemekezeka  Muhammad (s.a.a.w)  adamukhazikitsa  ndikumulengezetsa  Ali (a)  kuti  ndi mlowammalo    pambuyo  pake  popanda  kupezeka  munthu  wina  pakati  pawo.

cndikulitenga  kukhala  tsiku  la  lapamwamba  ndi  laulemerero  monga  mmene  tikumvera  mu  ma aya ali mmusiwa:
وَإِذْ أَخَذَ اللَّـهُ مِيثَاقَ النَّبِيِّينَ لَمَا آتَيْتُكُم مِّن كِتَابٍ وَحِكْمَةٍ ثُمَّ جَاءَكُمْ رَسُولٌ مُّصَدِّقٌ لِّمَا مَعَكُمْ لَتُؤْمِنُنَّ بِهِ وَلَتَنصُرُنَّهُ قَالَ أَأَقْرَرْتُمْ وَأَخَذْتُمْ عَلَىٰ ذَٰلِكُمْ إِصْرِي قَالُوا أَقْرَرْنَا قَالَ فَاشْهَدُوا وَأَنَا مَعَكُم مِّنَ الشَّاهِدِينَ ﴿آل عمران: ٨١﴾
وَإِنَّ مِن شِيعَتِهِ لَإِبْرَاهِيمَ ﴿الصافات: ٨٣﴾
Koma  kweni kweni  nkhani  ngati  imeneyi  amene  angathe  kuimvetsetsa   ndi  munthu  amene   ali  ndichikhulupiriro cha  Ahlubait, ndiye  ngati munthu  amene  Sali  muchikhulupirirochi   angamvetsetse  ndiye  kuti  kuyamikidwa  konse  ndikwa  Mulungu.
Nkhani   imeneyi ya  Ghadir  yomwe  ili  yofunikira  kwambiri  pakati  asilamu  chifukwa  choti  ikutifotokozera  kufunikira  kwa  kupitirira   chipembedzo  cha  chisilamu   pambuyo pa Mtumiki wathu  (s.a.a.w.)  kudzera  mwa  atsogoleri  okwana   khumi  ndi awiri (12)  omwe ali  ochokera  mwa  Mtumiki(s.a.a.w), tikuipeza  mu bukhu  lopatulika  la  Baibulo  pomwe  Ibrahim (a)  adalikulongosola  kwa  ana  ake Ishaq  ndi  Ismail  za  atumiki  omwe  adzabwere  pambuyo  pawo  kuti  kuchokera  kwa  Ismail  kudzabwera   atsogoleri  okwana  khumi  ndi awiri(12).
Pali  Riwayat   lomwe   likunena  kuti  Imam  Swadiq(a)   adafunsidwa  kuti  kodi  asilamu ali  ndichisangalalo  china  posakhala   lachisanu,  Qurubani  ndi   Fitir? Imam  Swadiq  adayankha  kuti  inde,  pali  chisangalalo  chomwe   chili  chapamwamba  kuposa   zisangalalo  zonse,  ofunsa  adati:  nditsiku liti  limeneli? Imam  adati:  nditsiku lomwe  Mtumiki(s.a.a.w)  adamupanga  Ali (a)  kukhala  mlowammalo  wake pambuyo  pake  ndipo  adalengeza  kwa anthu  onse  ponena  kuti yemwe  ine  Mtumiki(s.a.a.w)  ndidali  tsogoleri ndi  bwana  wake  adziwe ndikuvomereza  kuti  uyu  Ali (a)  ndi tsogolweri  komanso bwana  wake, tsikuli  lidali  pa 18 dthul hijah. Munthuyu  adati:  kodi  ndintchito  zanji   yomwe  tingapange  tsikuli? Imam  adayankha  kuti  muyenera  kusala, kupembedza, kumukumbukira  Mtumiki(s.a.a.w)  ndi  akunyumba  kwake ndikuwafunira  mafuno  abwino  ndi mtendere, litengeni  tsikuli  kukhala  lachisangalalo  chifukwa  Mtumiki  adamulangiza   Ali  kukhala  kuti  azilitenga  tsikuli  kukhala lachisangalalo. Angakhale  atumiki ena  adali  kuwalangiza  alowammalo  awo  kuti  tsiku  ngati  limeneli  aziltenga  kukhala  lachisangalalo.
Hadith  ina  yachokera  kwa  Ibn  Abi Nasir Bazantiy   yomwe  adainena  kuchokera kwa   Imam  Ridtha(a)  kuti  Imam  adanena  kwa  iye kuti  e!  iwe  mwana  wa  Abi  Nasir,  kwina  kuli konse  komwe  ungakhale likafika  tsiku la  chisangalalo  cha Ghadir uziyetsetsa  kukafika  ku manda  olemekezeka  a  Amir muminina  Ali (a)  chifukwa  tsiku  limeneli   Mulungu  amakhululuka  machimo   a munthu  okhulupirira wamwamuna  kapena  wamkazi   omwe  adawapanga  zaka  makumi asanu  ndi  limodzi (60), amamupulumutsa   kuchokera  ku moto  kuposa  momwe  adamupulumutsira  mu mwezi  wa Ramadthan, usiku  wa mphamvu (laylatul qadir)  ndi  usiku  wa  eidul fitir,  Kupereka  ndalama  zokwana  diriham  imodzi  kwa  m’bale  okhulupirira   tsiku limeneli  kuli  ndi ubwino  okwana   madiriham  chikhwi  chimodzi  kuposa  kupereka  masiku ena, uyenera  kuchitira  zabwino  ndi zosangalatsa  m’bale  okhulupirira  tsikuli  mwamuna  kapena  mkazi, ndikulumbira  mwa  Mulungu  kuti   zidakakhala  kuti  anthu  ubwino  watsikuli  amaudziwa   monga  momwe  zikufunikira  kuti  adziwe  ndiye kuti  angelo   adzakhala  akugwirana  nawe  dzanja  kakhumi  patsiku.
Chomwe  tiyenera  kudziwa  pankhaniyi  ndichoti  tiyenera  kupanga  zinthu  zosonyeza  kuti  tsikuli ndilalikulu.
Ntchito  zomwe  zili  zofunikira  kuzichita  tsikuli  ndi  izi:
1. kusala  komwe  mphoto  yake  ndichikhululuko  cha  machima  omwe  udawapanga  zaka  zokwana  makumi  asanu ndi limodzi.
2. kusamba.
3. Kumuyendera  Amir  uminina  Ali(a)  kukaona  manda  ake,  ndizabwino  kuti  munthu  ayenera  kuyetsetsa  kukafika  ku manda  ake  oyerawa.  Pali  ziyara  ya mitundu  itatu  yomwe  tikuipeza  mumariwaya; yoyamba ndiyomwe  imatchedwa  “amin allah” yomwe  itha  kusomedwa  pafupi  kapena   kutali. 
4. kupemphera  pemphero  la  maraka  awiri, ndipo  ikatha  muyenera  kupita  pa  sajidah(  kuika  mphumi  pansi)  ndikuthokoza  Mulungu  kokwana  ka  zana (100), kenako muweramuka  kuchokera  pa  sajidah  ndikukhala  ndikunena  dua  iyi:
اَللّهُمَّ اِنِّى اَسْئَلُكَ بِاَنَّ لَكَ الْحَمْدَ وَحْدَكَ لا شَريكَ لَكَ وَاَنَّكَ
E! ambuye  Mulungu,  ine   ndikukupemphani  inu  chifukwa  choti  ndinu  mwini  matamando  onse   komanso   palibe  wina  yemwe  tingamupembedze  muchoonadi  koma inu  nokha ndipo  mulibe  othandizana  naye  mu Umulungu  wanu
Mtumiki  olemekezeka (s.a.a.w)  adali  kulongosola  ubwino  omwe Msilamu  angapeze  ngati  atapanga  ntchito za  tsikuli, choncho  ankafika polongosola  upamwamba  wake  iye.  Nthawi  zina iye  akafuna  kuzilongosola  amalongosola  ubwino ndi upamwamba wa  Ali (a), mwachoncho  zimakhala  ngati  akuzilongosola  mwini  wake  chifukwa  choti  Ali  Mphunzitsi  wake  wamkulu ndi  iye  Mtumiki.
Ma Shaikh  ena  Ahlu sunnah wal jama’a  adanena  hadith  yomwe  ikuti:  tsiku lina  Mtumiki  adafunsidwa  kuti  kodi  munthu  yemwe  ali  wapamwamba  kuposa  iye  ndindani? Mtumiki  adayankha  kuti  Abubakar  ndi  Umar. Fatwimatu  Zahrah (a)  adafunsa  kuti  nanga  Ali  bwanji?  Mtumiki  adati: kodi  Ali  ndi ine  pali  kusiyana? Kusonyeza  kuti  anthu  awiri  amenewa  akubwera  pambuyo pa  Mtumiki  ndi  Ali. Kodi  ngati  Mtumiki(s.a.a.w) akumulongosola  Ali  ndi  upamwamba  otere  nanga  mwini  wake  ali  bwanji?
واحِدٌ اَحَدٌ صَمَدٌ لَمْ تَلِدْ وَلَمْ تُولَدْ وَلَمْ يَكُنْ لَكَ كُفُواً اَحَدٌ وَاَنَّ
Inu  amene  muli  nokha  komanso  mmodzi  ndipo  simufunikira  china  chilichonse,  inu  amene  mulibe  mwana  komanso  simunachite  kuberekedwa, palibe  chinthu  chomwe  chingafanane  nanu.
Tanthauzo  la Wahid  ndi  Ahad  ndiye  kuti  monga  mmene  chilili  cholembera  kuti  nthawi  yomwe  chisanalembe  china chilichonse chimakhala  kuti  mwa iye  zonse  zomwe  zalembedwazi ( inki yomwe  yatulutsidwa  ndikupanga  bukhu)  idalipo  ndipoyamba  pomwe  sikuti  yapezeka  nthawi  yomwe  lalembedwa  bukhu  ayi, kumasulira  kuti  Mulungu  ndi iye  yekhayo  yemwe  adalipo  ndiponso  pambuyo  pakupezeka  zopezeka  ndimmodzi  yekha  yemwe  ali  ndimphamvu  zopezeketsa  izozi  choncho  palibe  kunenenso  kuti  Mulungu  ali  ndichiyambi,  komanso  Mulungu  popanga  chinthu  sizifunikira  pakhale  chiyambi  chake  koma  kuti iye  ndi  amene  ali  opezekeza  zonsezi, iye  ndimwini  kupezeka  zopezeka  zonse.
       مُحَمّداً عَبْدُكَ وَرَسُولُكَ صَلَواتُكَ عَلَيْهِ وَ الِهِ يا مَنْ هُوَ كُلَّ يَوْمٍ فى

Ndithudi  Muhammad(s.a.a.w) ndi  kapolo  wanu  komanso Mtumiki  wanu ( mtendere  wanu  ukhale  kwa  iye   ndi akubanja  kwake, e!  Inu  amene tsiku  lina  lililonse  mumakhala  otanganidwa  ndi  ntchito   
شَاْنٍ كَما كانَ مِنْ شَاْنِكَ اَنْ تَفَضَّلْتَ عَلَىَّ بِاَنْ جَعَلْتَنى مِنْ اَهْلِ
ndipo  chifukwa cha  ntchito  zanu  zabwino  mwandipatsa  ine  mtendere  otha  kukhala 
اِجابَتِكَ وَاَهْلِ دِينِكَ وَاَهْلِ دَعْوَتِكَ وَوَفَّقْتَنى لِذلِكَ فى مُبْتَدَءِ
Munthu  ovomereza  chifuniro,  chipembedzo, kuitana  kwanu  ndipo  mudandikwaniritsira  zonse  kumayambiriro kwa  chilengedwe  changa
خَلْقى تَفَضُّلاً مِنْكَ وَكَرَماً وَجُوداً ثُمَّ اَرْدَفْتَ الْفَضْلَ فَضْلاً وَالْجُودَ
Zonsezi  chifukwa  cha  ubwino, mtendere,kupereka mowolowa manja  ndikukoma  mtima  kwanu  kenako  pambuyo  pa  ubwino
 mwabweretsanso  ubwino  wina, pambuyo  pa kupereka mowolowa manja  mwabweretsanso  kuolowa  manja  kwina o
Mtendere  umenewu  ndikupezeka  kwa  Mtumiki(s.a.a.w),  Ali, Hasan  ndi  Husain  omwe  ali  atsogoleri  pambuyo  pa  Mtumiki,  Mulungu  ndiodziwa  kukhonza  ndikuika chinthu  china  chilichonse  mofunikira  kuti  akapolo  ake  athe  kugwiritsa  ntchito  mwachitsanzo  Mulungu  adapanga  madzi  omwe  adapangidwa  ndi  zinthu  ziwiri  hydrogen  ndi  oxygen  kukhala  othandiza  munthu muzinthu  zina  ndi  zina,  koma hydrogen  yemweyo  akangogwiritsidwa  ntchito payekha  amasanduka  kukhala  owopsa  kwa  munthu monga  amatha  kuotcha  chimodzi-modzi  oxygen  koma  ataphatikiza  mukupezeka  mpumulo kuchokera mu  iwo
جُوداً وَالْكَرَمَ كَرَماً رَاْفَةً مِنْكَ وَرَحْمَةً اِلى اَنْ جَدَّدْتَ ذلِكَ الْعَهْدَ
Zonsezi  chifukwa  cha chifundo  ndichisoni  chanu  mwakutero  mwabwerezanso  lonjezo
لى تَجْديداً بَعْدَ تَجديدِكَ خَلْقى وَكُنْتُ نَسْياً مَنْسِيّاً ناسِياً ساهِياً
langa  pambuyo  poti  mwabwezeretsa  ndikukhonzanso  chilengedwe change  pamene  ine mwini  wanga  ndidali  oiwala  ndikuiwalidwa  komanso osazindikira  chilichonse,

غافِلاً فَاَتْمَمْتَ نِعْمَتَكَ بِاَنْ ذَكَّرْتَنى ذلِكَ وَمَنَنْتَ بِهِ عَلَىَّ وَهَدَيْتَنى

mwakwaniritsa  mtendere  wanga  pondikumbutsa, kundipatsa mtendere komanso  mwandiongola
لَهُ فَليَكُنْ مِنْ شَاْنِكَ يا اِلهى وَسَيِّدى وَمَولاىَ اَنْ تُتِمَّ لى ذلِكَ وَلا
Ndipo  chifukwa  cha ubwino  ndi ntchito   zanu  zabwino  ndikwaniritsireni  ine  mtendere  umenewu  e! inu  bwana  ndi  Mulungu  wanga,
تَسْلُبَنيهِ حَتّى تَتَوَفّانى عَلى ذلِكَ وَاَنتَ عَنّى راضٍ فَاِنَّكَ اَحَقُّ
Musandilande  mtendere  omwe  mwandaipatsawu  mpaka  kuti  mudzanditenge  ndidakali  mu iwo  ndipo  inu  muli  osangalala  nane.
Asakani  yemwe  ndi mwini  wa  bukhu lotchedwa  “Shawahid tanzil”, akunena  kuti  tanthauzo la  “mustaqim”  ndi  Ali(a). Kusonyeza  kuti  munthu  akhale  muchiongoko  ndikupeza  mtendere  ngati  umenewu  akufunikira  kuti  akhale  otsatira  njira  ya  Ali (a). Inde, tiyenera  kupempha  Mulungu  kuti  tisachoke  mubwato  limeneli  la  ahlubait (a)  chifukwa  pali  zitsanzo  zina  zomwe  zidapatsidwa  mtendere  ngati  umenewu  koma  mapeto  ake  adaluza.  Kodi  satana  sadali  munthu  wamkulu, nanga  Qaruna  sadalinso  munthu  wamkulu  koma  tapeza  onsewa  kuti  adagonja  ndikugwa  pansi  komanso  kutulutsidwa   mumtendere  wa  Mulungu,  choncho ife nthawi  zonse   pempho  lathu  lizikhala  loti  tisadzatuluke  mu mtendere  umenewu  kufikira  nthawi  yomwe  Mulungu  adzatitenge.
 المُنعِمينَ اَنْ تُتِمَّ نِعمَتَكَ عَلَىَّ اَللّهُمَّ سَمِعْنا وَاَطَعْنا وَاَجَبْنا داعِيَكَ 
Inu  ndi opereka  mtendere  weniweni  pachifukwachi  ndinu  amene  mungakwaniritse  mtendere  wanga, ambuye  Mulungu,    chifukwa  cha  chifundo chanu tamva,tamvera  ndipo  tavomera  oitanira  wanu,
بِمَنِّكَ فَلَكَ الْحَمْدُ غُفْرانَكَ رَبَّنا وَاِلَيكَ المَصيرُ امَنّا بِاللّهِ وَحدَهُ لا
Matamando  onse  ali  kwa  inu  ndipo  tikupempha  chikhululuko  chanu  e!  inu  bwana  wathu  ndipo  kwa inu  ndikobwerera,  ife  takhulupirira  mwa  Mulungu  mmodzi  yekha  
   شَريكَ لَهُ وَبِرَسُولِهِ مُحَمَّدٍ صَلَّى اللّهُ عَلَيْهِ وَ الِهِ وَصَدَّقْنا وَاَجَبْنا
Yemwe  alibe  othandizana  naye  mu Umulungu  wake  komanso  Mtumiki  wake  olemekezeka  Muhammad (s.a.a.w) pomuvomereza  ndikumuyankha  zomwe  adabwera  nazo
داعِىَ اللّهِ وَاتَّبَعْنَا الرَّسوُلَ فى مُوالاةِ مَوْلينا وَمَوْلَى الْمُؤْمِنينَ اَميرِ
 Komanso  oitanira  munjira  ya  Mulungu, tamutsatira  Mtumiki  wathu mu ubale  ndikumvera  tsogoleri  wanthu  ndi tsogoleri  wa  anthu  okhulupirira,
المُؤْمِنينَ عَلِىِّ بْنِ اَبيطالِبٍ عَبْدِاللّهِ وَاَخى رَسوُلِهِ وَالصِّدّيقِ الاْكْبَرِ
Ali  bin Abi Twalib (a)  yemwe  ndi kapolo  wa Mulungu  komanso  nzake  wa  Mtumiki(s.a.a.w) ndi odalilika  wamkulu,
وَالحُجَّةِ عَلى بَرِيَّتِهِ المُؤَيِّدِ بِهِ نَبِيَّهُ وَدينَهُ الْحَقَّ الْمُبينَ عَلَماً لِدينِ
Komanso  mboni  kwa  zolengedwa zake ndipo  Mtumiki ndi  chipembedzo chake choonadi chowonekera  paderachi  chidalimbikitsidwa  ndi iye  amenenso  ali mbendera ya  chipembedzo
اللّهِ وَخازِناً لِعِلْمِهِ وَعَيْبَةَ غَيْبِ اللّهِ وَمَوْضِعَ سِرِّ اللّهِ وَاَمينَ اللّهِ عَلى
Cha  Mulungu, nkhokwe  ya nzeru zake  ndi  zobisika  za  Mulungu komanso  odalilika  wake  pakati  pa  zolengedwa  zake,
خَلْقِهِ وَشاهِدَهُ فى بَرِيَّتِهِ اَللّهُمَّ رَبَّنا اِنَّنا سَمِعْنا مُنادِياً يُنادى
Mboni  mu zolengedwa  zake, e!  ambuye  Mulungu  amene  muli  bwana  wathu ife  tamumva  oitanira  kwa  inu akuitana 
للا يمانِ اَنْ امِنُوا بِرَبِّكُمْ فَامَنّا رَبَّنا فَاغْفِرْ لَنا ذُنُوبَنا وَكَفِّرْ عَنّا
Kuitanira  kuchikhulupiriro  ndicholinga  choti  tikhulupirire  ndipo  ife  takhulupirira  choncho  ambuye  Mulungu  tikhululukireni  machimo  athu 

سَيِّئاتِنا وَتَوَفَّنا مَعَ الاْبْرارِ رَبَّنا وَ اتِنا ما وَعَدْتَنا عَلى رُسُلِكَ وَلا
Ndipo  mutitenge  ife  tidakali  anthu  abwino  komanso  tipatseni  zinthu  zomwe  mudatilonjeza  kudzera   mwa  Mtumiki  wanu  olemekezeka
تُخْزِنا يَوْمَ الْقِيمَةِ اِنَّكَ لا تُخْلِفُ الْميعادَ فَاِنّا يا رَبَّنا بِمَنِّكَ وَلُطْفِكَ
musadzatichititse  manyazi  tsiku  lomaliza  ndithu  inu  simuononga  lonjezo  lanu, ife  chifukwa  cha  ubwino  ndi  chifundo  chanu 
اَجَبْنا داعِيَكَ وَاتَّبَعْنَا الرَّسُولَ وَصَدَّقْناهُ وَصَدَّقْنا مَوْلَى الْمُؤْمِنينَ
tavomera  kuitana  komwe  amaitanira  oitanira  wanu, tatsatira  Mtumiki wanu ndikumukhulupirira komanso  tsogoleri  wa  okhulupirira
وَكَفَرْنا بِالجِبْتِ وَالطّاغُوتِ فَوَلِّنا ما تَوَلَّيْنا وَاحْشُرْنا مَعَ اَئِمَّتِنا فَاِنّا
Ife  takanira  anthu  ozikweza  ndi odumpha  malire (anthu  omwe adalanda  udindo kuchokera  kwa  iye) choncho  tipangeni  ife  kukhala  pansi pa  ulamuliro  wake  monga  momwe  ife  tafunira  kuti  tikhale  mu ulamuliro  wake ndipo  mudzatizutse  kuchokera  mmanda  ndi  atsogoleri  athu  amenewa
Imam  Swadiq (a)  adanena  kuti  ngati  munthu  angachikonde  chinthu  angakhale   mwala  tsiku  lomaliza  adzadzukitsidwa nawo. Choncho  munthu amene  angawakonde  akunyumba  kwa Mtumiki(s.a.a.w)   ndiye  kuti tsiku  lomaliza  adzaukitsidwa  nawo
بِهِمْ مُؤْمِنُونَ مُوقِنُونَ وَلَهُمْ مُسَلِّمُونَ امَنّا بِسِرِّهِمْ وَعَلانِيَتِهِمْ
Chifukwa  ife  takhulupirira  mwa iwo ndikugonjera, takhulupirira  angakhale  zinthu  zobisika  ndi zoonekera  zawo   zomwe,
وَشاهِدِهِمْ وَغائِبِهِمْ وَحَيِّهِمْ وَمَيِّتِهِمْ وَرَضينا بِهِمْ اَئِمَّةً وَقادَةً
Anthu  opezeka  pakati  pawo  ndi  osapezeka, amoyo  awo  ndi  okufa, ndipo  tasangalala  ndi iwo  pakukhala  kwawo  atsogoleri, 
وسادَةً وَحَسْبُنا بِهِمْ بَيْنَنا وَبَيْنَ اللّهِ دُونَ خَلْقِهِ لا نَبْتَغى بِهِمْ بَدَلاً وَلا

Iwowa  atikwanira  kukhala  atsogoleri  athu  pakati  pathu  ndi  Mulungu  ndipo  sitikufuna  ena  mmalo  mwawo
نَتَّخِذُ مِنْ دُونِهِمْ وَليجَةً وَبَرِئْنا اِلَى اِلله مِنْ كُلِّ مَنْ نَصَبَ لَهُمْ حَرْباً
ndipo  sitingamulowetse  wina  mmitima  mwathu, tithawira  kwa  Mulungu  kuchokera   kwa  anthu  omwe   adakhazikitsa  kwa  iwo  nkhondo,
مِنَ الْجِنِّ وَالاِنْسِ مِنَ الاْوَّلينَ وَالاْ خِرينَ وَكَفَرْنا بِالْجِبْتِ
Kuchokera  majini, anthu oyambirira  ndi  omalizira  ndipo  takanira  anthu ozikweza,

وَالطّاغُوتِ وَالاَوثانِ الاَرْبَعَةِ وَاَشْياعِهِمْ وَاَتْباعِهِمْ وَكُلِّ مَنْ

Opsola  malire, mafano anayi, owatsatira  awo   ndi  ena  onse
والاهُمْ مِنَ الْجِنِّ وَالاِنْسِ مِنْ اَوَّلِ الدَّهرِ اِلى آخِرِهِ اَللّهُمَّ اِنّا
Omwe  ali pansi  pa ulamuliro  wawo  kuyambira ziwanda  ndi anthu  pachiyambi  mpaka  pamathero, e! ambuye  Mulungu,
نُشْهِدُكَ اَنّا نَدينُ بِما دانَ بِهِ مُحَمَّدٌ وَ الُ مُحَمَّدٍ صَلَّى اللّهُ عَلَيْهِ
Ife  tikuikira  umboni  kuti  takhala anthu  opembedza  monga  momwe  amapembedzera  Muhammad(s.a.a.w)  ndi  akunyumba  kwake(a),
وَعَلَيْهِمْ وَقَوْلُنا ما قالُوا وَدينُنا ما دانُوا بِهِ ما قالُوا بِهِ قُلْنا وَما دانُوا
Zolankhula  zathu  ndizokhazo  zomwe  iwo  amalankhula,  chipembedzo  chathu  ndichomwecho  chipembedzo  chawo, zomwe  adanena   tanena  ndipo  kupembedza  kwawo ndikomwe  tikupembedza
بهِ دِنّا وَما اَنْكَرُوا اَنْكَرْنا وَمَنْ والَوْا والَيْنا وَمَنْ عادَوْا عادَيْنا وَمَنْ
Zomwe  adazikanira  tazikanira,  omwe  adawakonda  ifenso  tawakonda,  omwe  adawada  tawadanso,
لَعَنُوا لَعَنّا وَمَنْ تَبَرَّؤُا مِنْهُ تَبَرَّاْنا [مِنْهُ] وَمَنْ تَرَحَّمُوا عَلَيْهِ تَرَحَّمْنا
omwe adawatemberera tawatembereranso, omwe  adazitalikitsa  kuchokera  kwa  iwo  ifenso  tazitalikitsa  kuchokera  kwa  iwo, omwe  adawachitira  chisoni  ifenso  tawachitira  chisoni,
عَلَيْهِ آمَنّا وَسَلَّمْنا وَرَضينا وَاتَّبَعْنا مَوالِيَنا صَلَواتُ اللّهِ عَلَيْهِمْ
Ife  takhulupirira,tagonjera,tasangalala ndiponso  tatsatira  atsogoleri  athu (mtendere  wa Mulungu  ukhale  kwa  iwo),
اَللّهُمَّ فَتَمِّمْ لَنا ذلِكَ وَلا تَسْلُبْناهُ وَاجْعَلْهُ مُسْتَقِرّاً ثابِتاً عِنْدَنا وَلا
e!  ambuye  Mulungu  tikwaniritsireni  ife  zinthu zimenezi   ndipo  musatilande  koma  muzipange  zimenezi  kukhala  zokhazikika  ndi zolimba  kwa  ife,
تَجْعَلْهُ مُسْتَعاراً وَاَحْيِنا ما اَحْيَيْتَنا عَلَيْهِ وَاَمِتْنا اِذا اَمَتَّنا عَلَيْهِ الُ

Musazipange  zinthuzi  kukhala  za nthawi  yochepa  kapena  zongobwerekera, tipatseni  ife  moyo  tidakali  ndi  zinthuzi  monga  momwe  mudawapatsira  akunyumba  ya  Mulungu(s.a.a.w)  ndi  izo,
مُحَمَّدٍ اَئِمَّتُنا فَبِهِمْ نَاْتَمُّ وَاِيّاهُمْ نُوالى وَعَدُوَّهُمْ عَدُوَّ اللّهِ نُعادى
Omwe  ndi  atsogoleri  athu  amene  timawatsatira  ndikuwakonda, adani  awo  omwenso  ndi  adani  a Mulungu  timawada,
فَاجْعَلْنا مَعَهُمْ فِى الدُّنْيا وَالاَّخِرَةِ وَمِنَ الْمُقَرَّبينَ فَاِنّ ا بِذ لِكَ ر اضُونَ
Tipangeni  ife  kukhala  limodzi   ndi  iwo  pano  pa dziko lapansi  ndi tsiku  lomaliza  komanso  kukhala  anthu  oyandikana nanu  chifukwa  ife  tili  osangalala  ndi zimenezi.
يا اَرْحَمَ الرّاحِمينَ
E!  inu  amene  muli  achisoni  kuposa  achisoni  onse.
Kenako  mupitanso  pa sajidah  ndikunena  mau oti “ Alhamudulillah” ndi “ Shukuranilillah”  kokwana  kazana.
Zidanenedwa  kuti  munthu  yemwe  angapange  ntchito  zomwe  zili zoyenera  kuzichita  tsiku limeneli  la  Ghadir  ndiye   kuti  adzakhala  ngati kuti  adali limodzi  ndi  Mtumiki(s.a.a.w)  tsiku  la  Ghadir, wagwirana  chanza  naye  komanso ali  limodzi  ndi  Imam  Zaman  mu mnyumba  mwake.
Nthawi  yabwino  kupemphera  pempheroli   ndi nthawi  yakuyandikira  kupendeka  kwa  dzuwa  chifukwa  ndi  nthawi  yomwe  Mtumiki(s.a.a.w)  adamukhazikitsa  Ali (a)  pa  ulowammalo  ndi utsogoleri  pambuyo  pake. Ndibwino  kuti  raka  yoyamba  asome  sura Qadir  ndi Tauhid  raka  yachiwiri.
Zikomo  kwambiri  Mulungu  akhale  nanu  ndikukupatsani  zabwino  za tsikuli.

 

Add new comment