Ndakatulo yokhudza Imam Husain(a)

Ndakatulo yokhudza  Imam  Husain(a)
 شیعتی ما ان شربتم ماء عذب فاذکرونی
اَو سَمعتم بغریب اَو شهید فَاندبونی
و انا سبط الذی من غیر جرم قتلونی
 وبجرد الخیل بعد القتل عمدا سحقونی
لیتکم فی یوم عاشورا جمیعا تنظرونی
کیف استسقی لطفلی فابوا ان یرحمونی
ویلهم قد  جرحوا قلب، لرسول الثقلین
فالعنوا هم ماستطعتم شیعتی فی کل حین
 شیعتی ما ان شربتم ماءَ عذبٍ فاذکرونی

Zochitika  zapa  Karbala  ndi  mavuto  akulu  kwambiri omwe  adagwa  muchisilamu.
Imam  Husain (a)  ataphedwa  thupi  lake  ndikugwera  pansi,  mau  adamveka kuchokera  mthupi lake  lomwe  lidali  loti  mutu  wake  udachotsedwa.  Kuchokera  muthupili  mudamveka  mau.  Mutu  wake  omwe  udaikidwa  kunsonga  kwa  nkondo  udali  kulankhula  mau  ndikuwerenga  Quran,  komanonso  thupi  lidalankhula  mau  omwe  ndindakatulo  yomwe  ili  mmwambayi.
Mauwa  adali  otere:
  شیعتی ما ان شربتم ماء عذب فاذکرونی
E! inu  onditsatira  anga ( mashia), nthawi  yomwe  mukumwa  madzi  ndikumbukireni  ine,  mukatero  inu  mukhala  mu shia  weni-weni.
Ndichifukwa  chake  nkhani  ikuti  Imam  Sajjad(a)  amati akaona  madzi  amalira  kwambiri,  amati  akafuna  kupanga  udthu ndikuona  madzi  amalira  kwambiri  mpaka  madzi  amasanduka amudthafu(madzi  oti  achoka  mulamulo  la  madzi monga  momwe    alili madzi  azipatso oti sizingatheke  kupangira  udthu).
Munthu  wina  adafunsidwa  kuti  kodi  ndintchito  yabwino  yanji  yomwe  wapanga  usiku  wa   Qadr,  iye  adayankha  kuti palibe  ntchito  yomwe  wapanga  kupatula  kuti  adangodzuka  ndikumwa  madzi  ndikumukumbukira  Imam  Husain(a), kudanenedwa  kwa  iye  kuti  wagwira  ntchito  yayikulu kwambiri  yomwe  mwini  wake  Husain  adaichemerera  monga  momwe tikumvera  mu ndakatuloyi.
Mfundo  yomwe  tingaunikirane  pamalopa  ndiyoti  tiyenera  kusiyanitsa  pakati  pandakatulo  zomwe  timazimva  zikunenedwa  ndi  anthu  ena  ndizomwe  anthu  ngati  Imam  Husain amanena.  Ndakatulo  zomwe  anthu  wamba  amakhala  akunena  zimakhala  zongosangalatsa  kapena  kupereka  phunziro  lina  lake pang’ono  pomwe  ndakatulo  za  anthu monga  Imam  Husain  ndichoonadi  chokha chokha  komanso  chiphunzitso  chachikulu  kwa  anthu.Mau   a anthu amenewa  alibe  chikaiko  mkati  mwake, ngati  inu  mumamva  mau awo  ndikukhala  ndichikaiko  dziwani  kuti  mumtima  mwanu  mulibe  chikondi  ndikhulupiriro  cha  akunyumba  kwa  Mtumiki(Ahlubait). Chifukwa  anthu  amenewa  akuchokera  mnyumba  mwa  Mtumiki(s.a.a.w)  amene  samalankhula  zinthu  zammutu  mwake  koma  amalankhula  zochokera  kwa  Mulungu. لا ينطق عن الهوى ان هو الاّ وحي يوحى
Mukamuyang’ana  Imam  Husain(a)  mumpeza  kuti  ndi  munthu  yemwe  ali  ndi ulemelero  waukulu. Anthu  omwe  bambo  ndi  mai  awo  awiri  ndi  ma’asum (ochinjirizidwa  ku  kuchima)  ndi  Hasan  ndi  Husain(a) .  Kusonyeza  kuti  Husain  sadali  munthu  wamba  oti  ndikumufanizira  ndi  Yazid  pa ubwino  ndi  upamwamba.
اَو سَمعتم بغریب اَو شهید فَاندبونی
Mukamva  zinthu  zodabwitsa  ndi  zovuta  komanso  kuphedwa  kwa  anthu  ena  ndikumbukireni  ndikundidandaulira.
Mukaona  zodabwitsa  ndi  mavuto  (monga  mmene  anthu  ambiri  akuphedwera,  ana,  nkhalamba  ndi  anthu  odwala  ku Miyanmar,Pakistan,Afghanistan, Iraq  ndi  ena)  ndikumanidwa  madzi,  kumbukirani  kuti  zinthu  zimenezi  ndizomwe  zidandionekera  ine  Husain  choncho   khalani  odandaula  ndi izo.
 و انا سبط الذی من غیر جرم قتلونی
Ine  ndi chidzukulu  chomwe  chidaphedwa  popanda  tchimo  lina  lililonse.
Anthuni  kutheka  kuti  mwina  inu  simukundidziwa  kuti  ine  ndindani,  ndikuuzani,  ine  ndi chidzukulu  cha  Mtumiki  wa  Mulungu (s.a.a.w)  chomwe  anthu  oponderezawa  adachipha  popanda  tchimo.Kodi  inu  mungandiuze  kuti  kodi  Imam  Husain  adamupheranji?  Husain  ndi:
- Chidzukulu  cha  Mtumiki  wa Mulungu.
- Mtumiki  adanena  za  iye  kuti  ndichikongoletso cha  chindanda  cha  Mulungu.
- Bwana  wa  anyamata  a kumtendere.
- Mtumiki  adati :حسين مني وانا من الحسين  ((Husain ochokera  mwa  ine,  inenso  ochokera  mwa  iye))
- Ndi  mwini  wa  aya  ya Mawaddah.
- Ndi  mwini  wa  aya  ya Mubahalah.
- Ndi  mwini  wa  sura ya Hal-ata.
Nthumwi  ina  yaku Rome  yomwe  idakhala  nawo  pa msonkhano  wa  Yazid  idati  kwa  iye:  iwe  Yazid  chipembedzo changa  chili  bwino  kuposa  chipembedzo  chako   chifukwa  ine  ndichidzukulu  cha  mmodzi  mwa  atumuki  koma  ndimalemekeza  atumiki  ndi  azibale  onse  komanso  sindinapange  zomwe  iwe  wapanga  popha  mwana  wa  Mtumiki  wanu  ndikumasangalala  chonchi.
 Palibe  chifukwa  chomwe  inu  mungachitchule  chomveka  chomwe  mudamuphera  Husain kupatula  chikhulupiriro  chake  choyera mu chisilamu.

وبجرد الخیل بعد القتل عمدا سحقونی
Munandipondaponda  ndi  hachi  pambuyo  pakundipha dala.
Chifukwa  chimodzi  chomwe  chidachititsa  kuti  Imam  Husain asaikidwe  mmanda  nthawiyo  chidali  choti  thupi  lake  lidali  loti  lanyenyeka-nyenyeka  chifukwa  choliponda- ponda  ndi  hachi.
Pambuyo  pakupha  Imam  Husain (a)  Umar bin Saad  adakuwa  kuti  kodi  ndi ndani  yemwe  angaponde-ponde  thupi  la  Husain  kuti  akalandire  mphoto  yayikulu?  Kudapezeka  anthu  okwana  khumi  omwe  adazipereka  kuti  agwira  ntchito  imeneyi,  mmodzi  wawo  adali  Usaid  bin Malik  yemwe  atafika  kwa  Ubaidullah bin  Ziyad  adali  kulongosola  monyadira  kuti  ndife  amene  taponda-ponda  thupi  la  Husain(a).
لیتکم فی یوم عاشورا جمیعا تنظرونی
Tsoka  likhale  kwa  inu  chifukwa  cha  zomwe  mwachita  tsiku  limeneli  la pa 10  mwezi  wa  Muharram  pondipha  ine  uku  mukuyanga’nira  mavuto  anga.
Anthu  amenewa  mitima  yawo  idalimba  kuposa  mwala  posaganizira  angakhale  pang’ono mavuto omwe  angakumane  nawo pambuyo  pakupha  chidzukulu  cha  Mtumiki(s.a.a.w) , kodi  iwowa  adalibe  manyazi  kuti  akakumana  ndi  Mtumiki  wawo  akamuyang’ana  ndi khope  yotani  komanso  akamuuza  chani  za  Husain(a). Iyayi,  satana  akamupanika  munthu  pomutalikitsa  ndichilungamo  ndichoonadi  zimakhala  monga  chonchi.
کیف استسقی لطفلی فابوا ان یرحمونی
Ndizotheka  bwanji  kuti  ine  ndipemphe  madzi  a  mwana  wanga  koma  ndikukana  kundipatsa  osandimvera  chisoni.
Chisilamu  ndichipembedzo  chomwe  chimatiphunzitsa  nkhani  ya  chisoni  kufikira  pomwe  chikunena  kuti  ngati  munthu  utakhala  muchipululu  ndipo  uli  ndi  madzi  ochepa  okwanira  kupangira  udthu,  ngati  patabwera  chinyama  chaludzu  akuti  madziwo  uchipatse  chinyamacho  iwe upange  tayammam,  ichi  ndichisilamu  chomwe  ife  tikuchidziwa,  tsono  anthu  amenewa  chisilamu  chawo ndichotani  chopanda  chisoni  angakhale  kwa  mwana  wang’ono  yemwe  kumukaniza  madzi? Chisilamu  chawo  ndichamtundu  wanji  chopanda  chisoni  kwa  munthu  wapamwamba  ngati  Husain(a)  mpaka  kumukaniza  madzi?  Ine   chisilamu  cha  iwowa  chikundidabwitsa  kwambiri. Husain  (a)  nkhani  itafika  pothina  adanena  kwa  iwo  kuti:
منّوا على ابن المصطفى اما ترونه كيف  يتلظى عطشانا؟
Muchitireni  chifundo  mwana  wa Muhammad Musitafah,  kodi  inu  simukuona  momwe  akuvutikira  ndi ludzu?
Munthu  yemwe  angamukumbukire  Imam  Husain(a)  nthawi  yomwe  akumwa  madzi  mphoto  yake  ndi  yoti:
- Adzakhala  ngati  adali limodzi  ndi  Imam  Husain(a)  ku karibala ,adaphedwa  naye limodzi.
- Adzakhala  ngati  kuti  wapereka  madzi  kwa  ana  aludzu   a Imam  Husain(a)  .
Imam  Husain adalankhula  kwa  Shimr  kuti:
يا شمر! اذا  كان لابدّ  من قتلي فاسقني جرءة  من الماء
E! Shimr,  ngati  watsimikiza  zofuna  kundipha  ine  ndipatseko  madzi  pang’ono.
Imam  Husain(a)  adalikufuna  kumukumbutsa  Shimr  kuti  mwina  akumbukira  ndikubwerera  mwa  Mulungu  ndicholinga  choti  mawa  asadzanene  kuti  sindimadziwa  chilichonse. Chifukwa  Mulungu  ndiokhululuka.
 

ویلهم قد  جرحوا قلب، لرسول الثقلین
Tsoka  likhale  kwa  iwo  chifukwa  choti adavulaza  mtima  wa  Mtumiki wa zinthu  ziwiri  zolemera ( anthu  ndi  majini).
Mtumiki (s.a.a.w) adali  kumukonda  Imam  Husain(a)  ndipo  tsiku  lina  adali  kumupsopsona  kwambiri  kufikira  poti  adamufunsa  kuti  kodi  zimenezi  akupangilanji.  Mtumiki  adati: ndikupsopsona  malo   omwe  mivi  ndi  mikondo  idzakhala  ikufikira.
Chabwino  zomwe  mukufuna  kupangazo  pangani,  anawo  iphani, akaziwo  vutitsani,  asilikali  angwiro  a Husain  iphani,  chidzukulu  cha  Mtumiki  omalizachi  iphani  koma  dziwani  kuti  Mulungu, Mtumiki  ndi  anthu  okhulupirira  adzaona  ntchito zanuzo.  قل اعملوا سيرى الله عملكم و رسوله و المؤمنون

 

Add new comment