Ashura mukuyang’ana kwa Akirisitu
Ashura mukuyang’ana kwa Akirisitu
Talongosola mmbuyomu kuti tikamati Ashura timatanthauza tsiku lomwe Husain mwana wa Ali chidzukulu cha Mtumiki(s.a.a.w) chidaphedwa. Nkhaniyi ndiyoti mu history ilipo ndipo idakhazikika angakhale munthu wina atafuna kuti aibise sizingatheke, koma mmalo mwake tikupeza kuti angakhale akirisitu adavomereza za nkhaniyi kuti Imam Husain (a) adaphedwa moponderezedwa pofuna kuteteza chisilamu kuchokera kwa anthu omwe amafuna kuthimitsa kuwala kwake. Ena mwa akirisitu akulankhula motere:
1. Charlez Dikenz (Mlembi otchuka waku England) adanena kuti: ngati cholinga cha Imam Husain(a) pomenyana ndi adani chidali kufuna za dziko lapansi, chimene ine sindikumvetsa ndichoti chifukwa chani iye adatenga azilongo,ana ndi akazi ake? Poona zimenezi nzeru zanga zikunena kuti iye adapanga izi chifukwa cha chisilamu basi.
2.Thomas Carloil (Philosopher ndi historian waku England) adati: Chiphunzitso chomwe tikuchipeza muzochitika zodandaulitsa za pa Karbala ndi zoti Imam Husain(a) ndi anthu ake adali anthu okhulupirira Mulungu ndipo olimba pofuna kuteteza chipembedzo cha Mulungu. Zomwe adapanga iwo zidaonetsera poyera nkhani yakusiyana kwa pakati pa chilungamo ndi bodza ndipo kupambana kwake angakhale kuti adali ndi anthu ochepa kwandidabwitsa kwambiri.
3.Edward Brown ( Orientalist waku England) adati: kodi pali mtima omwe ungakhale osadandaula ndikumva kuwawa pambuyo pomva nkhani yomwe idachitika ku Karbala? Angakhale anthu omwe sali Asilamu sangathe kukanira kuyera mtima kwa munthu(Husain) yemwe adamenya nkhondo ya chisilamu imeneyi.
4.Fredrick James adati: Phunziro la Imam Husain komanso munthu wina aliyense yemwe angafere munjira ya Mulungu ndiloti padziko lino lapansi pali zinthu zamuyaya zomwe zilipo zoti mkati mwake muli chisoni,chifundo ndi chikondi zomwe sizingasinthe choncho munthu yemwe angalimbane ndi gulu lina lake pofuna kuchinjiriza chinthu china chake chomwe ndichamtengo wapatali zinthu zimenezi zimatsalira padziko lino lapansi.
5.Washington Irewing (Historian otchuka waku America) akuti: Kudali kotheka kuti Imam Husain(a) apulumutse moyo wake pogonjera zofuna za Yazid, koma chifukwa cha udindo wa tsogoleri ndi chiphunzitso cha chisilamu pa nkhani ya kulimbana ndi anthu oukira icho (Jihad) sizidapereke mwai kwa Imam Husain(a) kuti amuvomere Yazid kuti ndi mtsogoleri wa Asilamu (Khalifah) koma kuti iye adalolera mavuto ndi mazunzo onse mmalo mosiya chisilamu mmanja mwa mabani umayyah. Tiyenera kudziwa kuti mzimu wa Husain udakalipo pansi pa dzuwa lowotcha ndi malo ouma (karbala). Kusonyeza kuti zotsatira za nkhondo imeneyi ndikupambana kwa Imam Husain yemwe anthu ma million lero lino amakhala akumukumbukira angakhale omwe sali Asilamu pongoona kuyera kwa cholinga chake.
6.Thomas Mosoric adati: Angakhale kuti akulu akulu ansembe amasintha mitima ya anthu kufika podandaula kwambiri potchula mavuto okhudza Issah(a) koma kudabwitsa ndikuzinzwa kwa zomwe Husain ndi asikali ake adachita sikungapezeke mu mavuto a Issah ndipo mavuto a Issah ali ngati kamwala kakang’ono komwe kaima molingana ndi phiri lalikulu.
7. Morris Dukbary adati: malo omwe amasonkhana ndikumakumbukira mavuto a Husain amanena kuti Husain adalimbana ndi Yazid posavomera zofuna zake ndicholinga chofuna kuteteza kulemekezeka, ulemu wa anthu ndi chipembedzo cha chisilamu. Choncho adalolera kuti chuma chake, moyo wake ndi ana ake zionongedwe bola ateteze zinthuzi. Tatiyeni ifenso tigwiritse ntchito njira ya Husain imeneyi polimbana ndi anthu opondereza chifukwa choti imfa yolemekezeka ili bwino kuposa imfa yonyozeka.
8. Marbin( odziwa nkhani zapa middle east waku Germany) adati: Zomwe adachita Husain popereka anthu okondedwa ake adatsimikizira za kuponderezedwa kwake komanso uchowona wake. Iye adaphunzitsa dziko lonse lapansi nkhani yakuzipereka ndipo adakhazikitsa chisilamu ndikufalitsa dzina lake ndi Asilamu. Msilikali olungamayu adauza dziko lapansi kuti kupondereza kulibe nthawi yotalika ayi angakhale kuti kuoneke ngati kuli ndi mphamvu koma kumauluka ndiphepo mosakhalitsa.
9. George Jurdock ( munthu ophunzira chilankhulo) akuti: Yazid atawauza anthu ndikuwalimbikitsa kuti aphe Husain, iwo adali kumufunsa kuti mutipatsa ndalama zochuluka bwanji? Koma asilikali a Husain adali kunena kwa iye kuti ife tili nawe angakhale tiphedwe kokwana kakhumi ndi kasanu ndi kawiri (70) tikhalabe mu gulu lako mpaka timenye nkhondo ndikuphedwa. Kodi kusiyana kumeneku kukuchokera pati?
10. Anttony Bara adati: adakakhala Husain(a) wa ife (mkirisitu) tidakaika malo ena alionse mbendera yake ndipo mmudzi wina ulionse tidakakhazikitsa tchalitchi ndikumaitanira anthu mudzina lake.
M’bale olemekezeka awa ndi akirisitu omwe atha kuona ndikuzindikira choonadi chenicheni cha nkhani ya Imam Husain(a) yomwe idachitika pa Karbala, tsono iwe m’bale amene uli msilamu ukukanika bwanji kuimvetsetsa nkhaniyi?
Add new comment