Kugwiliridwa kwa mwana wa zaka zisanu ndi shaikh (mufut) wa chiwahabi wa ku Saud

 
mufut-wahabi- agwilirira-mwana-wake.

Kugwiliridwa  kwa  mwana  wa zaka  zisanu  ndi  shaikh (mufut) wa chiwahabi wa ku Saud
Mkulu  wina  yemwe  amazitenga  kuti  ndi munthu  ophunzira  chipembedzo  cha   chisilamu  wa  chiwahabi  dzina  lake  Faihan Alghamidi   walamulidwa  kuti  akwapulidwe  zikwapu  zokwana   mazana  asanu  ndi  atatu (800)  ndikukakhala  kundende  zaka  zisanu  ndi  zitatu   chifukwa  chopezeka  olakwa  pa mlandu  ogwilirira  mwana  wamkazi  wazaka  zisanu mdziko  la  Saud  Arabia.
Mu kulankhula  kwa  Tv  Shia   nkhani  ikuti   mkuluyu  kuonjezera  pa  chilango  chomwe  walandira  wauzidwanso  kuti  alipire  ndalama  zokwana   1 million  Rial  Saudi  kukhala  ngati  chindapusa,  ndalama  zomwe  zikukwanira  270 Dollars. Pali chiyembekezo  choti  ndalamazi   ziperekedwa   kwa mai  amwanayu  yemwe  ndi  mkazi wake  wakale.
Mai  wa mwanayu  akufuna  kuti  mkuluyu  ayenera  kupereka  ndalama  zina  zokwana  10 million  Rial Saud   chifukwa  cha  imfa  ya mwanayu.  Mkazi  wachiwiri  wamkuluyu   yemwe  naye  akuzengedwa  mlandu  othandizira  mwamuna  wake  pankhaniyi   walamulidwa  kuti  akwapulidwe  zikwapu zokwana  150  ndikukakhala  kundende  zaka  zokwana  khumi.
Dzina  la  mwanayu  lidali  Lami   yemwe  adali  mwana  wake  mkuluyu ( kusonyeza  kuti  chitsiru  cha  bambo   ngati  ichi  chidagona  ndikugwilirira  mwana  wake)  yemwe  pa 25 December 2011  adamutengera  kuchipatala  atavulazidwa  kwambiri   pa nthawi  yomwe  mkuluyu  amamugwilirira, kenako  mukudutsa  kwa  miyezi  ingapo  mwanayu  adamwalira.
Tiyeni  azibambo  tikhale  achisoni  kwa  ana  athu.

 

Add new comment